Maranatha Global

The Spirit and the bride say, “Come!” – Rev. 22:17

Chichewa (Nyanja)

The main language of Malawi, parts of Zambia, parts of Zimbabwe, and parts of Mozambique. Approximately 10 million native speakers. Also called Chewa, Chinyanja, or Nyanja.

28
Aug

malawi5-150x14317KUKHALA CHOPHWEKA KOMA CHOYANG’ANITSITSA

1 Akorinto 1:17-23 – “Pakuti Khristu sanandituma ine kubatiza, koma kulalikira Uthenga Wabwino, si mu nzeru ya mawu, kuti mtanda wa Khristu ungayesedwe opanda pache.  Pakuti mawu a mtanda ali ndithu chinthu chopusa kwa iwo akutaika, koma kwa ife amene tikupulumutsidwa ali mphamvu ya Mulungu.  ….  koma ife talalikira Khritu wopachikidwa”

Tikuona mu vesi limeneli komanso vesi la m’mwamba kuchokera ku 1 Akorinto 2, Paulo sanasamale zosangalatsa anthu kapena kuonetsa chikhalidwe ngati wolalikira wa mkulu.  Sanagwiritse ntchito mawu kuti anthu amve ngati iye ndi wamzeru, ngakhale iye anakatha kuzichita izi bwino koposa wina aliyense, kupatsidwa chidwi chake kuphunzira ndi chikhalidwe chake ngati ophunzira.  Sanapereke zinthu zotiyenereza kukhala Mkhristu.  Kalalikidwe kake kanali kosavuta komanso koyang’ana kwa Yesu.  Iye anamvetsetsa kuti anthu akuyenera kukhala komanso kukumana ndi Yesu, kuphunzira za mphamvu ya mwazi wa Yesu komanso kuuka kwake.  Pamene anthu adziwa zinthu zimenezi Mzimu oyera udzafika ndikuyamba kulamulira.

continue

Tags : , , , , , , , , , , , , , , , , , , ,
Category : Chichewa (Nyanja) | Blog
28
Aug

malawi5-150x14317KULAKIRA KWA PAULO

1 Akorinto 2:2-4 “Ndipo mawu anga ndi kulalikira kwanga sanakhala ndi mawu okopa anzeru, koma m’chionetso cha Mzimu ndi champhamvu; kuti chikhulupiriro chanu chisakhale m’nzeru ya anthu, koma ya mu mphamvu ya Mulungu.  ”

Pali mawu ena amene munthu wina otchuka, Augustine Hippo ananena.  Iye anati: Pali zinthu zitatu zimene iye amafuna kuonetsetsa ndi maso ake, koma sanathe, “Ambuye Yesu mu nthawi ya utumiki wake padziko lapansi, wolamulira wamkulu wa ku Rome ndi kutchuka kwake ndi kulamulira kwa Paulo, momga olalikira opatsa chidwi komanso otchuka kwambiri, (ngati Augustine amene anali mphunzitsi waukachenjede asanasandulike) chifukwa Baibulo likutiuza zambiri za utumiki wake komanso zitsanzo zambiri mu malemba kuposa chiri chonse mu chipangano cha tsopano.  Inde, tikuona kuti Mulungu anakhazikitsa Paulo ngati chitsanzo kuti Akhristu titsatire pophatikizirapo  zitsanzo zambiri zimene zinali mu zolembera zake.  Paulo monga olalikira woyamba, maganizo amene amakhala ndi anthu ambiri zimakhala zosiyana ndi zimene Baibulo likunena pa kulalikira kwake.

continue

Tags : , , , , , , , , , , , , , , , , , , ,
Category : Chichewa (Nyanja) | Blog
28
Aug

malawi5-150x14317CHANGU CHA PAULO PAKUMVERA

Afilipo 2:5-7 “Mukhale nao mtima mkati mwanu umene unalinso mwa Khristu Yesu, ameneyo pokhala nao maonekedwe a Mulungu sanachiyese cholanda kukhala ofana ndi Mulungu, koma anadzikhuthula yekha natenga maonekedwe a ukapolo, nakhala mafanizidwe a munthu, ”

1 Akorinto 11:1 “Khalani onditsanza ine monga m’mene nditsanza ndi Khristu.  ”

M’madera ambiri amoyo wake, Paulo anakhazikitsa dongosolo la chikhakidwe chomwe samalimbana ndi okhulupirira ena amene amatsanzira.  Kudalira ku mphamvu zimene Mzimu Woyera anamupatsa iye kukagonjetsa zofuna za thupi lake, Paulo analimbikira kumutsanza Yesu Khristu.  Paulo anamvetsetsa mu zaka zimene Yesu anayenda ngati munthu pa dzik olapansi mu utumiki wake, anakanitsitsa kupanga kapena kuchita chiri chonse koma chokhacho chomwe chinamukondweretsa Tate wake.  Mwa njira imeneyi, pamene Yesu anadzitengera yekha “chikhalidwe cha kapolo” anatipatsa ife chitsanzo chooneka bwino m’mene zingaonekere pakuyang’anira chindunji pa kutumikira Mulungu.  Yesu anayankhula mawu okhawo ochokera kwa Atate.  Anachita zinthu zokhazo zomwe zinamukondweretsa Atate, ndipo sanalore chikhalidwe cha umunthu wake kutsogolera zomwe akunena ndi kuchita.

continue

Tags : , , , , , , , , , , , , , , , , , , ,
Category : Chichewa (Nyanja) | Blog
28
Aug

KUDZIPEREKA KWA PAULO KU MUYAYA

Akolose 3:1-4 “Chifukwa chake ngati munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, funani za kumwamba, kumene kuli Khristu okhala ku dzanja lamanja la Mulungu.  Lingalirani zakumwamba osati za padziko ai.  Pakuti munafa ndipo moyo wanu wabisika ndi Khristu mwa Mulungu.  Pamene Khristu adzaoneka, ndiye moyo wathu,  pamene inunso mudzaonekera pamodzi ndi Iye m’ulemerero.  ”

Chinthu chimodzi cha makalata amene Paulo amalemba amayang’ana pa muyaya.  Anthu ambiri masiku ano amaganiza za mtumwi Paulo monga mphumzitsi wamkulu kapena kuti odzala mipingo kapenanso munthu amene anapanga zinthu zodabwitsa zazikulu.  Zinthu zonsezi ndi zoona.  Koma tikamamuona Paulo mwini, timuona kuti anayesesa kufuna kukhazikitsa moyo wake pa Khristu komanso kufuna umuyaya wa Mulungu.

continue

Tags : , , , , , , , , , , , , , , , , , , ,
Category : Chichewa (Nyanja) | Blog
28
Aug

malawi5-150x14317MTHUNZI WA WAMPHAMVU YONSE Masalmo 91:1

“ Iye amene akhala pansi m’ngaka yace ya Wam’mwambamwamba, adzagonera mumthunzi wa Wamphanvu yonse”

Chigawo choyamba cha phunziroli, chikuyang’ana gawo loyamba la vesi limeneli, “Mthunzi wa Wam’mwambamwamba” ndipo chigawo chachiwiri chikuyang’ana mbali ina ya vesi lomweli.  (Ndime imeneyi ili ndi magawo awiri omwe mawu ake akuchokera mu Chihebri. )

KUPUMA: Mawu oyamba mu chigawo choyamba cha vesili, “Kukhala” kulodzera chisankho chomwe tayenera kupanga- kukhala chifupi ndi Mulungu mu thupi lake ndi muvumbulutso.

continue

Tags : , , , , , , , , , , , , , , , , , , ,
Category : Chichewa (Nyanja) | Blog
28
Aug

malawi5-150x14317

KULIKANIKIZA  KHUTU NDI CHITSEKO:  (Thrust his ear through the door)

Deutronomo 15:16-17 - “Ndipo kudzakhala, akanena ndi inu, Sindituluka kuchoka kwanu; popeza akonda inu ndi nyumba yanu, popeza kumkomera kwanu, pamenepa muzitenga lisungulo, ndikulipisa mkhutu mwache, kulikanikiza ndi chitseko, ndipo adzakhala kapolo wanu kosalekeza.  Muzichitanso momwemo ndi adzakazi anu”

Izi zikukamba za atumiki komanso akapolo mu chipangano chakale, koma kufotokozera m’mene tikukhalira atumiki a Ambuye masiku ano.  Pali goli lofanana ndi dongosolo lache pa Eksodo 21:2-6.  Aisraeli amayenera kumasula kapolo wawo wa chiHebri kapena mtumiki wina aliyense akagwira ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri.  Ngakhale zinali chonchi, atumiki amakhalabe mu udindowo mokhazikika ngati anafuna kutero.  Chiyankhulo cheni cheni cha Baibulo sichinasiyanitse pakati pa kapolo ndi mtumiki monga timachitira mu chingerezi.

continue

Tags : , , , , , , , , , , , , , , , , , , ,
Category : Chichewa (Nyanja) | Blog
28
Aug

malawiBULU NDI CHOIKAPO CHAKE (Donkey and the Saddle)

Marko 11:1-7, Matt. 21

“Ndipo anati kwa iwo, pitani pa mudzi wa pandunji nanu; mukangolowa m’menemo mudzapeza mwana wa bulu.

continue

Tags : , , , , , , , , , , , , , , , , , , ,
Category : Chichewa (Nyanja) | Blog
28
Aug

malawiKUDIKIRA NGONGOLE (CHIKOLE)

“Mukakongoletsa mnasi wanu ngongole iri yonse, musamalowe nyumba mwake kudzitengera chikole chake.  Muima pa bwalo, ndi munthu amene amkongoletsayo adzituluka nacho chikolecho kwa inu muli pabwalo.  ”

CHIYAMBI: Monga gawo limene lafotokozedwa kuti wobwereketsa akuyenera kudikira pakhomo pa yemwe wabwerekayo, chomwecho chipangano chatsopano chikuti Yesu akudikira pa khomo la miyoyo yathu, kudikirira ife.  “Ine ndiri pano! Ndaima pakhomo ndipo ndigogoda.  ” Chivumbulutso 3:20.  Ichi ndi chikonzero cha chinenero chomwe ife ochimwa tikuyenera kulumikizana ndi Yesu polandira cholowa cha chipulumutso chake.  Yesu ndi amene ali ndi chiri chinso chomwe tifuna- chikhululukiro kumachimo, kubadwa mwatsopano, vumbulutso la Mzimu Woyera, mphatso za Mzimu, kuyeretsa komanso zina zambiri.  Timabwera kwa Iye pamene tikufuna chiri chonse.  Mwatokha, mu thupi lathu, palibe china chiri chonse chimene timafuna kwa muyaya.

continue

Tags : , , , , , , , , , , , , , , , , , , ,
Category : Chichewa (Nyanja) | Blog
25
Aug

malawiNYIMBO YA SOLOMO GAWO LOYAMBA – Song Of Songs Part 1

Nyimbo ya Solomo 1 vs 1:3

Mnyamatayo andipsopsonetsa ndi m’kamwa mwache, pakuti chikondi chake chapeza vinyo, mafuta ako anunkhila bwino; Dzina lako likunga mafuta onunkhila bwino otsanulidwa.  ”

MAU OYAMBA:

Solomo ndi chizindikilo cha Mzimu Oyera, makamaka mzimu omwe ukulamulila mu mpingo.  Mwa zonse Nyimbo ya Solomo ndi chinenero cha mphamvu ndi ubale pakati pa Khristu ndi mpingo okhulupilira.

continue

Tags : , , , , , , , , , , , , , , , , , , ,
Category : Chichewa (Nyanja) | Blog
18
Apr
MZIMAYI WA KU SAMARIA: UTHENGA NDI BVUMBULUTSO: (The Samaritan Woman – Evangelism and Revelation)
Yohane 4: 16-19
“Yesu ananena kwa iye, Muka,  kayitane mwamuna wako nudze kuno.  Mkazi anayankha nati kwa Iye, ndilibe mwamuna.  Yesu ananena naye, Wanena bwino, kuti mwamuna ndiribe, pakuti wakhala nawo amuna asanu, ndipo Iye amene ukhale naye tsopano Sali mwamuna wako, ichi wanena zoona.  Mkazi ananena ndi Iye, Ambuye ndizindikira kuti mulu mneneri.”
Pali maphunziro ambiri omwe tingaphunzire kuchokera ku nkhani iyi ya Yesu ndi mzimayi wa ku Samaria.  Nkhaniyi ndi yodziwika bwino kwa anthu ambiri okhulupilira, Yesu alitu kudikira yekha pa chitsime (Chitsime cha Yakobo)  kunja kwa mudzi wa Samaria, ndipo pamene mzimayi akudza kudzatunga madzi, Yesu akumufunsa kuti amupatse madzi akumwa.  Mzimayiyu nthawi yomweyo anayamba kutsutsana naye nati kunali kosayenera kuti Iye angalankhulane naye.  Yesu ananena naye nati wataya mwayi opempha madzi a moyo.  Kuteroko sanamve kuti iyeyo ponena za bvumbulutso la muyaya, sanali kunena za madzi wamba ayi.  Kotero kuti anapitiriza kutsutsana naye.  Pomaliza Yesu anati iye anali ndi madzi opha ludzu kwa nthawi zonse.  Ndipo iye anapempha madziwo, kuti asadzapezenso madzi ena ku chitsimecho chifukwa chinali chi ntchito cholemetsa.
Iyi ndi nthawi yoyamba mzimayi kupempha madzi a moyowo.  Zikuyimira gawo loyamba lomwe munthu ayenera kutsata kuti afike kwa Ambuye.  Komabe   kumvetsa kwake  kunali koperewera.  Amaganiza za madzi omwe timamwa nthawi zonse ochokera pa chitsime.   Iye malingalira za momwe angapewere kupitapita ku chitsime.  Anthu osakhulupilira akayamba moyo omutsatira Yesu ndi kupemphera, amaganizirabe za momwe moyo wawo ungapindulire ku thupi.  Amayembekezera machilitso, chuma, kapena kumasulidwa ku chiyanjo china chake chosakhala bwino m’banja.  Amafuna kuthawa mabvuto ena a  m’moyo wao.  Izi sizachilendo, mwatsoka, ambiri amagomera pomwepo ndi kulephera kuyenda naye Ambuye, ndipo alaliki ena amasiya anthu adakali pa malo oterewa.
Osati Yesu.  Pamene mzimayiyu anapempha Iye, naye anayankha popempha chosowa chake: Pita ukayitane mwamuna wako, izitu zinabweresa kusokonezeka m’moyo wa mzimayiyu- Maukwati ake asanu olephera komanso moyo wake wa dama.  Iye sakumudzudzula kapena ku munyogodola.  Iyeyo akumufunsa kuchita chinthu cha pafupi, pamene akuyankha mwachidule, akumufotokozera nkhani yonse mwatsatane-tsatane.  Mwadzidzidzi akuzindikira kuti akulankhulana  ndi munthu wina wake wokhala ndi mau ochokera ku mwamba, mnenei kapena wina wake wotumidwa ndi mphamvu ya m’mwambamwamba.
Zonenedwa zake zonse zinali za uneneri, zokamba za mabvuto auzimu, oposa dama.   Faifi amayimira mautumiki asanu a m’baibulo, omwe amayimira mpingo okhulupirika, Mkwatibwi wa Khristu opatulika mu utumuki wa Yesu mu Mpingo (Aefeso 4:11- Atumwi, Aneneri, Alaliki, Abusa ndi Aphunzitsi).  M’malo mwake Yesu akuti, Ali ndi mwamuna wa chisanu ndi chimodzi.  Chisanu mchimodzi chimayimira munthu mu bukhu lopatulika: Adamu adalengedwa tsiku lachisanu ndi chimodzi, komanso otsutsana ndi Khristu amadziwika ndi nambala ya 666.  Ambuyetu tikuona apa akuphatikiza zonsezi munkhaniyi pofuna kufotokezera ife za bvuto lathu mu uzimu, osati kusankha kolakwikwa kwa mzimayiyu ayi.  Akufotokozera za onse omwe sali mwa Khristu kapena kukangamila pa mautumiki asanuwa, m’malo mwake moyo wao wauzimu wadzadza ndi ntchito za kuthupi.
Apa Yesu akupereka mau achidziwitso (1 Akorinto 12:8) Palibe wina aliyense ochokera m’mudzimu adakatha kudziwa za chinsinsi cha mzimayiyu.  Bvumbulutsoli lipambana malingaliro ake onse pakutsutsana kwake.  Zikupyora malingaliro ake onse a kuthupi omwe Khristu adakamuchitira iye.  Lero ichi ndi chinthu chofunika chomwe Yesu akuna kuti ife tikhale nacho pa utumiki wa kufalitsa uthenga.  Tiyenera kupemphera kuti tikhale naye muchiyanjano cha mabvumbulutso oterewa ndi mau ake a chidziwitso,  pamodzi ndi mphatso za uzimu.   Kudzichepetsa kotere kumafunika kwambiri  potumukira kusiyana ndi kudzikweza polalikira uthenga kuti ena atembenuke mtima.  Yesu sanadzikweze.  Sanazungulire ndi uthenga wake, kapena kufuulira, kapena kutsutsana naye.  Adatsiriza zonena zake ndi bvumbulutso la pafupi.
Posachedwa pa msonkhano wina, mzimayi wina adatsalira kuti apemphereredwe ndi abusa angapo.  Adawaonetsa chithunzi cha anyamata awiri, nati iwo adali ana ake ndipo m’modzi anali kufuna machiritso, pamene winayo ankafuna ntchito.  Nthawi yomweyo m’busa adalandira bvumbulutso lochokera kwa Ambuye: Amanama.  Adamuuza mosalimbana naye kuti mnyamata odwalayo anali atamwalira kale, ndipo kuti winayo sanali mwana wake weniweni.  Mzimayiyo anayamba kulira, navomereza kuti zinali zoona.  Mnyamatayo adali atamwalira miyezi ingapo yapitayo.  Winanayo anali wachibale chabe osati mwana wake.  Adaulura kuti adapititsa chithunzicho kumipingo yosiyanasiyana, komwe azibusa ambiri adamuuza kuti mwana odwalayo achiritsidwa (adali atamwalira kale), namati winayo adzapeza ntchito ndi zina zotere.  Koma atabwera kumapemphero kwathu ndiko kumene adakumana ndi Mulungu akulankhula chowonadi.  Izi ndizo timayembekezera alendo kukumana nazo.  Uthengawo ndi ofunikira kwambiri, komanso kupembedzera, koma mau achidziwitsowo amakhala maziko abwino a chikhulupiliro muchiyanjano  chawo ndi Khristu kwa nthawi zosatha.  Yesu yemweyo adazindikira zosowa za mzimayi wa ku Samaria ali moyo lero ndipo akulankhulabe ndi atumiki ake.  Izi zimatithandiza kufalitsa uthenga  wabwino munjira yomwe imabweretsa anthu   kwa Mulungu, ndikumufikira koposa kupeza zosowa zawo zonse, ndikuzindikira kuti Mulungu amadziwa zonse za mbuyo mwawo  ndipo afuna kusintha miyoyo yawo.

malawi5-150x14317MZIMAYI WA KU SAMARIA: UTHENGA NDI BVUMBULUTSO (The Samaritan Woman – Evangelism and Revelation)

Yohane 4: 16-19 - “Yesu ananena kwa iye, Muka,  kayitane mwamuna wako nudze kuno.  Mkazi anayankha nati kwa Iye, ndilibe mwamuna.  Yesu ananena naye, Wanena bwino, kuti mwamuna ndiribe, pakuti wakhala nawo amuna asanu, ndipo Iye amene ukhale naye tsopano Sali mwamuna wako, ichi wanena zoona.  Mkazi ananena ndi Iye, Ambuye ndizindikira kuti mulu mneneri.”

Pali maphunziro ambiri omwe tingaphunzire kuchokera ku nkhani iyi ya Yesu ndi mzimayi wa ku Samaria.  Nkhaniyi ndi yodziwika bwino kwa anthu ambiri okhulupilira, Yesu alitu kudikira yekha pa chitsime (Chitsime cha Yakobo)  kunja kwa mudzi wa Samaria, ndipo pamene mzimayi akudza kudzatunga madzi, Yesu akumufunsa kuti amupatse madzi akumwa.  Mzimayiyu nthawi yomweyo anayamba kutsutsana naye nati kunali kosayenera kuti Iye angalankhulane naye.  Yesu ananena naye nati wataya mwayi opempha madzi a moyo.  Kuteroko sanamve kuti iyeyo ponena za bvumbulutso la muyaya, sanali kunena za madzi wamba ayi.  Kotero kuti anapitiriza kutsutsana naye.  Pomaliza Yesu anati iye anali ndi madzi opha ludzu kwa nthawi zonse.  Ndipo iye anapempha madziwo, kuti asadzapezenso madzi ena ku chitsimecho chifukwa chinali chi ntchito cholemetsa.

continue

Tags : , , , , , , , , , , , , , , , , , , ,
Category : Chichewa (Nyanja) | Blog